< Masalimo 127 >
1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Salimo la Solomoni. Yehova akapanda kumanga nyumba, omanga nyumbayo agwira ntchito pachabe. Yehova akapanda kulondera mzinda, mlonda akanangolondera pachabe.
A Song of Ascents; of Solomon. Except the LORD build the house, they labour in vain that build it; except the LORD keep the city, the watchman waketh but in vain.
2 Mumangodzivuta nʼkulawirira mmamawa ndi kusagona msanga madzulo, kuvutikira chakudya choti mudye, pakuti Iye amapereka tulo kwa amene amawakonda.
It is vain for you that ye rise early, and sit up late, ye that eat the bread of toil; so He giveth unto His beloved in sleep.
3 Ana ndiye cholowa chochokera kwa Yehova, ana ndi mphotho yochokera kwa Iye.
Lo, children are a heritage of the LORD; the fruit of the womb is a reward.
4 Ana a pa unyamata ali ngati mivi mʼmanja mwa munthu wankhondo.
As arrows in the hand of a mighty man, so are the children of one's youth.
5 Wodala munthu amene motengera mivi mwake mwadzaza. Iwo sadzachititsidwa manyazi pamene alimbana ndi adani awo pa zipata.
Happy is the man that hath his quiver full of them; they shall not be put to shame, when they speak with their enemies in the gate.