< Masalimo 126 >
1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Yehova atabwezera akapolo ku Ziyoni, tinali ngati amene akulota.
Wimbo wa kwenda juu. Bwana alipowarejeza mateka Sayuni, tulikuwa kama watu walioota ndoto.
2 Pakamwa pathu panadzaza ndi kuseka; malilime athu ndi nyimbo zachimwemwe. Pamenepo kunanenedwa pakati pa anthu kuti, “Yehova wawachitira zinthu zazikulu.”
Vinywa vyetu vilijaa kicheko, ndimi zetu zilijaa nyimbo za shangwe. Ndipo iliposemwa miongoni mwa mataifa, “Bwana amewatendea mambo makuu.”
3 Yehova watichitira zinthu zazikulu, ndipo tadzazidwa ndi chimwemwe.
Bwana ametutendea mambo makuu, nasi tumejaa furaha.
4 Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova, monga mitsinje ya ku Negevi.
Ee Bwana, turejeshee watu wetu waliotekwa, kama vijito katika Negebu.
5 Iwo amene amafesa akulira, adzakolola akuyimba nyimbo zachimwemwe.
Wapandao kwa machozi watavuna kwa nyimbo za shangwe.
6 Iye amene amayendayenda nalira, atanyamula mbewu yokafesa, adzabwerera akuyimba nyimbo zachimwemwe, atanyamula mitolo yake.
Yeye azichukuaye mbegu zake kwenda kupanda, huku akilia, atarudi kwa nyimbo za shangwe, akichukua miganda ya mavuno yake.