< Masalimo 126 >
1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Yehova atabwezera akapolo ku Ziyoni, tinali ngati amene akulota.
Кад враћаше Господ робље сионско, бејасмо као у сну.
2 Pakamwa pathu panadzaza ndi kuseka; malilime athu ndi nyimbo zachimwemwe. Pamenepo kunanenedwa pakati pa anthu kuti, “Yehova wawachitira zinthu zazikulu.”
Тада уста наша беху пуна радости, и језик наш певања. Тада говораху по народима: Велико дело чини Господ на њима.
3 Yehova watichitira zinthu zazikulu, ndipo tadzazidwa ndi chimwemwe.
Велико дело чини Господ на нама; развеселисмо се.
4 Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova, monga mitsinje ya ku Negevi.
Враћај, Господе, робље наше, као потоке на сасушену земљу.
5 Iwo amene amafesa akulira, adzakolola akuyimba nyimbo zachimwemwe.
Који су са сузама сејали, нека жању с певањем.
6 Iye amene amayendayenda nalira, atanyamula mbewu yokafesa, adzabwerera akuyimba nyimbo zachimwemwe, atanyamula mitolo yake.
Иде и плаче који носи семе да сеје; поћи ће с песмом носећи снопове своје.