< Masalimo 126 >
1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Yehova atabwezera akapolo ku Ziyoni, tinali ngati amene akulota.
Pieśń stopni. Gdy PAN odwrócił niewolę Syjonu, byliśmy jak we śnie.
2 Pakamwa pathu panadzaza ndi kuseka; malilime athu ndi nyimbo zachimwemwe. Pamenepo kunanenedwa pakati pa anthu kuti, “Yehova wawachitira zinthu zazikulu.”
Wtedy usta nasze napełniły się śmiechem, a nasz język radością; wtedy mówiono między narodami: PAN uczynił wielkie rzeczy dla nich.
3 Yehova watichitira zinthu zazikulu, ndipo tadzazidwa ndi chimwemwe.
PAN uczynił dla nas wielkie rzeczy i z tego się radujemy.
4 Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova, monga mitsinje ya ku Negevi.
Odwróć, PANIE, naszą niewolę jak strumienie na południu.
5 Iwo amene amafesa akulira, adzakolola akuyimba nyimbo zachimwemwe.
Ci, którzy sieją we łzach, będą żąć z radością.
6 Iye amene amayendayenda nalira, atanyamula mbewu yokafesa, adzabwerera akuyimba nyimbo zachimwemwe, atanyamula mitolo yake.
Kto wychodzi z płaczem, niosąc drogie ziarno, powróci z radością, przynosząc swoje snopy.