< Masalimo 126 >
1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Yehova atabwezera akapolo ku Ziyoni, tinali ngati amene akulota.
Ingoma yemiqanso. Kwathi lapho uThixo ebuyisa izithunjwa eZiyoni, sasinjengabantu abaphuphayo.
2 Pakamwa pathu panadzaza ndi kuseka; malilime athu ndi nyimbo zachimwemwe. Pamenepo kunanenedwa pakati pa anthu kuti, “Yehova wawachitira zinthu zazikulu.”
Imilomo yethu yayigcwele ngohleko, lezindimi zethu zicula izingoma zentokozo. Basebesithi abezizwe, “UThixo ubenzele izinto ezimangalisayo.”
3 Yehova watichitira zinthu zazikulu, ndipo tadzazidwa ndi chimwemwe.
UThixo usenzele izinto ezimangalisayo, ngakho siyathokoza kakhulu.
4 Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova, monga mitsinje ya ku Negevi.
Buyisa ukuphumelela kwethu, Oh Thixo, njengemifula eseNegebi.
5 Iwo amene amafesa akulira, adzakolola akuyimba nyimbo zachimwemwe.
Labo abahlanyela ngezinyembezi bazavuna ngezingoma zentokozo.
6 Iye amene amayendayenda nalira, atanyamula mbewu yokafesa, adzabwerera akuyimba nyimbo zachimwemwe, atanyamula mitolo yake.
Lowo ophuma ekhala, ethwele inhlanyelo ukuba ayehlanyela uzabuya ngezingoma zentokozo, ethwele izinyanda.