< Masalimo 126 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Yehova atabwezera akapolo ku Ziyoni, tinali ngati amene akulota.
Canticum graduum. In convertendo Dominus captivitatem Sion: facti sumus sicut consolati:
2 Pakamwa pathu panadzaza ndi kuseka; malilime athu ndi nyimbo zachimwemwe. Pamenepo kunanenedwa pakati pa anthu kuti, “Yehova wawachitira zinthu zazikulu.”
Tunc repletum est gaudio os nostrum: et lingua nostra exultatione. Tunc dicent inter gentes: Magnificavit Dominus facere cum eis.
3 Yehova watichitira zinthu zazikulu, ndipo tadzazidwa ndi chimwemwe.
Magnificavit Dominus facere nobiscum: facti sumus laetantes.
4 Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova, monga mitsinje ya ku Negevi.
Converte Domine captivitatem nostram, sicut torrens in Austro.
5 Iwo amene amafesa akulira, adzakolola akuyimba nyimbo zachimwemwe.
Qui seminant in lacrymis, in exultatione metent.
6 Iye amene amayendayenda nalira, atanyamula mbewu yokafesa, adzabwerera akuyimba nyimbo zachimwemwe, atanyamula mitolo yake.
Euntes ibant et flebant, mittentes semina sua. Venientes autem venient cum exultatione, portantes manipulos suos.

< Masalimo 126 >