< Masalimo 126 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Yehova atabwezera akapolo ku Ziyoni, tinali ngati amene akulota.
Grádicsok éneke. Mikor visszahozta az Úr Sionnak foglyait, olyanok voltunk, mint az álmodók.
2 Pakamwa pathu panadzaza ndi kuseka; malilime athu ndi nyimbo zachimwemwe. Pamenepo kunanenedwa pakati pa anthu kuti, “Yehova wawachitira zinthu zazikulu.”
Akkor megtelt a szánk nevetéssel, nyelvünk pedig vígadozással. Akkor így szóltak a pogányok: Hatalmasan cselekedett ezekkel az Úr!
3 Yehova watichitira zinthu zazikulu, ndipo tadzazidwa ndi chimwemwe.
Hatalmasan cselekedett velünk az Úr, azért örvendezünk.
4 Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova, monga mitsinje ya ku Negevi.
Hozd vissza, Uram, a mi foglyainkat, mint patakokat a déli földön!
5 Iwo amene amafesa akulira, adzakolola akuyimba nyimbo zachimwemwe.
A kik könyhullatással vetnek, vígadozással aratnak majd.
6 Iye amene amayendayenda nalira, atanyamula mbewu yokafesa, adzabwerera akuyimba nyimbo zachimwemwe, atanyamula mitolo yake.
A ki vetőmagját sírva emelve megy tova, vígadozással jő elő, kévéit emelve.

< Masalimo 126 >