< Masalimo 126 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Yehova atabwezera akapolo ku Ziyoni, tinali ngati amene akulota.
שִׁיר הַֽמַּעֲלוֹת בְּשׁוּב יְהוָה אֶת־שִׁיבַת צִיּוֹן הָיִינוּ כְּחֹלְמִֽים׃
2 Pakamwa pathu panadzaza ndi kuseka; malilime athu ndi nyimbo zachimwemwe. Pamenepo kunanenedwa pakati pa anthu kuti, “Yehova wawachitira zinthu zazikulu.”
אָז יִמָּלֵא שְׂחוֹק פִּינוּ וּלְשׁוֹנֵנוּ רִנָּה אָז יֹאמְרוּ בַגּוֹיִם הִגְדִּיל יְהוָה לַעֲשׂוֹת עִם־אֵֽלֶּה׃
3 Yehova watichitira zinthu zazikulu, ndipo tadzazidwa ndi chimwemwe.
הִגְדִּיל יְהוָה לַעֲשׂוֹת עִמָּנוּ הָיִינוּ שְׂמֵחִֽים׃
4 Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova, monga mitsinje ya ku Negevi.
שׁוּבָה יְהוָה אֶת־שבותנו שְׁבִיתֵנוּ כַּאֲפִיקִים בַּנֶּֽגֶב׃
5 Iwo amene amafesa akulira, adzakolola akuyimba nyimbo zachimwemwe.
הַזֹּרְעִים בְּדִמְעָה בְּרִנָּה יִקְצֹֽרוּ׃
6 Iye amene amayendayenda nalira, atanyamula mbewu yokafesa, adzabwerera akuyimba nyimbo zachimwemwe, atanyamula mitolo yake.
הָלוֹךְ יֵלֵךְ ׀ וּבָכֹה נֹשֵׂא מֶֽשֶׁךְ־הַזָּרַע בֹּֽא־יָבוֹא בְרִנָּה נֹשֵׂא אֲלֻמֹּתָֽיו׃

< Masalimo 126 >