< Masalimo 126 >
1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Yehova atabwezera akapolo ku Ziyoni, tinali ngati amene akulota.
Waƙar haurawa. Sa’ad da Ubangiji ya dawo da kamammu zuwa Sihiyona, mun kasance kamar mutanen da suka yi mafarki.
2 Pakamwa pathu panadzaza ndi kuseka; malilime athu ndi nyimbo zachimwemwe. Pamenepo kunanenedwa pakati pa anthu kuti, “Yehova wawachitira zinthu zazikulu.”
Bakunanmu sun cika da dariya, harsunanmu da waƙoƙin farin ciki. Sai ana faɗi a cikin al’ummai, “Ubangiji ya aikata manyan abubuwa dominsu.”
3 Yehova watichitira zinthu zazikulu, ndipo tadzazidwa ndi chimwemwe.
Ubangiji ya aikata manyan abubuwa dominmu, mun kuwa cika da farin ciki.
4 Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova, monga mitsinje ya ku Negevi.
Ka maido da wadatarmu, ya Ubangiji kamar rafuffuka a Negeb.
5 Iwo amene amafesa akulira, adzakolola akuyimba nyimbo zachimwemwe.
Waɗanda suka yi shuka da hawaye za su yi girbi da waƙoƙin farin ciki.
6 Iye amene amayendayenda nalira, atanyamula mbewu yokafesa, adzabwerera akuyimba nyimbo zachimwemwe, atanyamula mitolo yake.
Shi da ya fita yana kuka, riƙe da iri don shuki, zai dawo da waƙoƙin farin ciki, ɗauke da dammuna.