< Masalimo 126 >
1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Yehova atabwezera akapolo ku Ziyoni, tinali ngati amene akulota.
Une chanson d'ascension. Lorsque Yahvé ramena ceux qui étaient revenus à Sion, nous étions comme ceux qui rêvent.
2 Pakamwa pathu panadzaza ndi kuseka; malilime athu ndi nyimbo zachimwemwe. Pamenepo kunanenedwa pakati pa anthu kuti, “Yehova wawachitira zinthu zazikulu.”
Et notre bouche s'est remplie de rires, et notre langue avec des chants. Alors on dit parmi les nations, « Yahvé a fait de grandes choses pour eux. »
3 Yehova watichitira zinthu zazikulu, ndipo tadzazidwa ndi chimwemwe.
Yahvé a fait de grandes choses pour nous, et nous sommes heureux.
4 Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova, monga mitsinje ya ku Negevi.
Rétablis notre fortune, Yahvé, comme les ruisseaux du Néguev.
5 Iwo amene amafesa akulira, adzakolola akuyimba nyimbo zachimwemwe.
Ceux qui sèment dans les larmes récolteront dans la joie.
6 Iye amene amayendayenda nalira, atanyamula mbewu yokafesa, adzabwerera akuyimba nyimbo zachimwemwe, atanyamula mitolo yake.
Celui qui s'en va en pleurant, portant de la semence pour semer, reviendra certainement avec joie, portant ses gerbes.