< Masalimo 126 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Yehova atabwezera akapolo ku Ziyoni, tinali ngati amene akulota.
A Song of Ascents. When the LORD turned again the captivity of Zion, we were like unto them that dream.
2 Pakamwa pathu panadzaza ndi kuseka; malilime athu ndi nyimbo zachimwemwe. Pamenepo kunanenedwa pakati pa anthu kuti, “Yehova wawachitira zinthu zazikulu.”
Then was our mouth filled with laughter, and our tongue with singing: then said they among the nations, The LORD hath done great things for them.
3 Yehova watichitira zinthu zazikulu, ndipo tadzazidwa ndi chimwemwe.
The LORD hath done great things for us; [whereof] we are glad.
4 Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova, monga mitsinje ya ku Negevi.
Turn again our captivity, O LORD, as the streams in the South.
5 Iwo amene amafesa akulira, adzakolola akuyimba nyimbo zachimwemwe.
They that sow in tears shall reap in joy.
6 Iye amene amayendayenda nalira, atanyamula mbewu yokafesa, adzabwerera akuyimba nyimbo zachimwemwe, atanyamula mitolo yake.
Though he goeth on his way weeping, bearing forth the seed; he shall come again with joy, bringing his sheaves [with him].

< Masalimo 126 >