< Masalimo 126 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Yehova atabwezera akapolo ku Ziyoni, tinali ngati amene akulota.
“A psalm of the steps, or the goings up.” When the LORD brought back the captivity of Zion, We were like them that dream.
2 Pakamwa pathu panadzaza ndi kuseka; malilime athu ndi nyimbo zachimwemwe. Pamenepo kunanenedwa pakati pa anthu kuti, “Yehova wawachitira zinthu zazikulu.”
Then was our mouth filled with laughter, And our tongue with singing. Then said they among the nations, “The LORD hath done great things for them!”
3 Yehova watichitira zinthu zazikulu, ndipo tadzazidwa ndi chimwemwe.
Yea, the LORD hath done great things for us, For which we are glad.
4 Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova, monga mitsinje ya ku Negevi.
Bring back, O LORD! our captivity, Like streams in the South!
5 Iwo amene amafesa akulira, adzakolola akuyimba nyimbo zachimwemwe.
They who sow in tears Shall reap in joy.
6 Iye amene amayendayenda nalira, atanyamula mbewu yokafesa, adzabwerera akuyimba nyimbo zachimwemwe, atanyamula mitolo yake.
Yea, he goeth forth weeping, bearing his seed; He shall surely come back rejoicing, bearing his sheaves.

< Masalimo 126 >