< Masalimo 126 >
1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Yehova atabwezera akapolo ku Ziyoni, tinali ngati amene akulota.
A Song of Ascents. When the LORD brought back those that returned to Zion, we were like unto them that dream.
2 Pakamwa pathu panadzaza ndi kuseka; malilime athu ndi nyimbo zachimwemwe. Pamenepo kunanenedwa pakati pa anthu kuti, “Yehova wawachitira zinthu zazikulu.”
Then was our mouth filled with laughter, and our tongue with singing; then said they among the nations: 'The LORD hath done great things with these.'
3 Yehova watichitira zinthu zazikulu, ndipo tadzazidwa ndi chimwemwe.
The LORD hath done great things with us; we are rejoiced.
4 Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova, monga mitsinje ya ku Negevi.
Turn our captivity, O LORD, as the streams in the dry land.
5 Iwo amene amafesa akulira, adzakolola akuyimba nyimbo zachimwemwe.
They that sow in tears shall reap in joy.
6 Iye amene amayendayenda nalira, atanyamula mbewu yokafesa, adzabwerera akuyimba nyimbo zachimwemwe, atanyamula mitolo yake.
Though he goeth on his way weeping that beareth the measure of seed, he shall come home with joy, bearing his sheaves.