< Masalimo 126 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Yehova atabwezera akapolo ku Ziyoni, tinali ngati amene akulota.
A song of degrees, or Psalme of David. When ye Lord brought againe the captiuitie of Zion, we were like them that dreame.
2 Pakamwa pathu panadzaza ndi kuseka; malilime athu ndi nyimbo zachimwemwe. Pamenepo kunanenedwa pakati pa anthu kuti, “Yehova wawachitira zinthu zazikulu.”
Then was our mouth filled with laughter, and our tongue with ioye: then sayd they among the heathen, The Lord hath done great things for them.
3 Yehova watichitira zinthu zazikulu, ndipo tadzazidwa ndi chimwemwe.
The Lord hath done great things for vs, whereof we reioyce.
4 Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova, monga mitsinje ya ku Negevi.
O Lord, bring againe our captiuitie, as the riuers in the South.
5 Iwo amene amafesa akulira, adzakolola akuyimba nyimbo zachimwemwe.
They that sowe in teares, shall reape in ioy.
6 Iye amene amayendayenda nalira, atanyamula mbewu yokafesa, adzabwerera akuyimba nyimbo zachimwemwe, atanyamula mitolo yake.
They went weeping and caried precious seede: but they shall returne with ioye and bring their sheaues.

< Masalimo 126 >