< Masalimo 126 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Yehova atabwezera akapolo ku Ziyoni, tinali ngati amene akulota.
A Song of degrees. When Jehovah turned the captivity of Zion, we were like them that dream.
2 Pakamwa pathu panadzaza ndi kuseka; malilime athu ndi nyimbo zachimwemwe. Pamenepo kunanenedwa pakati pa anthu kuti, “Yehova wawachitira zinthu zazikulu.”
Then was our mouth filled with laughter, and our tongue with rejoicing: then said they among the nations, Jehovah hath done great things for them.
3 Yehova watichitira zinthu zazikulu, ndipo tadzazidwa ndi chimwemwe.
Jehovah hath done great things for us; [and] we are joyful.
4 Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova, monga mitsinje ya ku Negevi.
Turn our captivity, O Jehovah, as the streams in the south.
5 Iwo amene amafesa akulira, adzakolola akuyimba nyimbo zachimwemwe.
They that sow in tears shall reap with rejoicing:
6 Iye amene amayendayenda nalira, atanyamula mbewu yokafesa, adzabwerera akuyimba nyimbo zachimwemwe, atanyamula mitolo yake.
He goeth forth and weepeth, bearing seed for scattering; he cometh again with rejoicing, bearing his sheaves.

< Masalimo 126 >