< Masalimo 126 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Yehova atabwezera akapolo ku Ziyoni, tinali ngati amene akulota.
When Jehovah brought back those who returned to Zion, we were like those who dream.
2 Pakamwa pathu panadzaza ndi kuseka; malilime athu ndi nyimbo zachimwemwe. Pamenepo kunanenedwa pakati pa anthu kuti, “Yehova wawachitira zinthu zazikulu.”
Then our mouth was filled with laughter, and our tongue with singing. Then they said among the nations, Jehovah has done great things for them.
3 Yehova watichitira zinthu zazikulu, ndipo tadzazidwa ndi chimwemwe.
Jehovah has done great things for us. We are glad.
4 Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova, monga mitsinje ya ku Negevi.
Turn again our captivity, O Jehovah, as the streams in the South.
5 Iwo amene amafesa akulira, adzakolola akuyimba nyimbo zachimwemwe.
Those who sow in tears shall reap in joy.
6 Iye amene amayendayenda nalira, atanyamula mbewu yokafesa, adzabwerera akuyimba nyimbo zachimwemwe, atanyamula mitolo yake.
He who goes forth and weeps, bearing seed for sowing, shall doubtless come again with joy, bringing his sheaves.

< Masalimo 126 >