< Masalimo 126 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Yehova atabwezera akapolo ku Ziyoni, tinali ngati amene akulota.
Der Herren hjemførte Zions Folk, som vendte tilbage, da vare vi som drømmende,
2 Pakamwa pathu panadzaza ndi kuseka; malilime athu ndi nyimbo zachimwemwe. Pamenepo kunanenedwa pakati pa anthu kuti, “Yehova wawachitira zinthu zazikulu.”
da blev vor Mund fyldt med Latter og vor Tunge med Frydesang, da sagde man iblandt Hedningerne: Herren har gjort store Ting imod disse.
3 Yehova watichitira zinthu zazikulu, ndipo tadzazidwa ndi chimwemwe.
Herren har gjort store Ting imod os; vi bleve glade.
4 Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova, monga mitsinje ya ku Negevi.
Hjemfør, Herre! vore fangne, lig Sydlandets Strømme.
5 Iwo amene amafesa akulira, adzakolola akuyimba nyimbo zachimwemwe.
De, som saa med Graad, skulle høste med Frydesang.
6 Iye amene amayendayenda nalira, atanyamula mbewu yokafesa, adzabwerera akuyimba nyimbo zachimwemwe, atanyamula mitolo yake.
Den, som bærer Sæden, der saas, gaar sin Gang med Graad; men han skal komme med Frydesang, naar han hjembærer sine Neg.

< Masalimo 126 >