< Masalimo 126 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Yehova atabwezera akapolo ku Ziyoni, tinali ngati amene akulota.
Píseň stupňů. Když zase vedl Hospodin zajaté Sionské, zdálo se nám to jako ve snách.
2 Pakamwa pathu panadzaza ndi kuseka; malilime athu ndi nyimbo zachimwemwe. Pamenepo kunanenedwa pakati pa anthu kuti, “Yehova wawachitira zinthu zazikulu.”
Tehdážť byla plná radosti ústa naše, a jazyk náš plésání; tehdáž pravili mezi národy: Veliké věci s nimi učinil Hospodin.
3 Yehova watichitira zinthu zazikulu, ndipo tadzazidwa ndi chimwemwe.
Učinilť jest s námi veliké věci Hospodin, a protož veselili jsme se.
4 Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova, monga mitsinje ya ku Negevi.
Uvediž zase, ó Hospodine, zajaté naše, tak jako potoky na vyprahlou krajinu.
5 Iwo amene amafesa akulira, adzakolola akuyimba nyimbo zachimwemwe.
Ti, kteříž se slzami rozsívali, s prozpěvováním žíti budou.
6 Iye amene amayendayenda nalira, atanyamula mbewu yokafesa, adzabwerera akuyimba nyimbo zachimwemwe, atanyamula mitolo yake.
Sem i tam chodící lid s pláčem rozsívá drahé símě, ale potom přijda, s plésáním snášeti bude snopy své.

< Masalimo 126 >