< Masalimo 125 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Amene amadalira Yehova ali ngati phiri la Ziyoni, limene silingagwedezeke koma ndi lokhala mpaka muyaya.
Надеющиися на Господа, яко гора Сион: не подвижится в век живый во Иерусалиме.
2 Monga mapiri azungulira Yerusalemu, momwemonso Yehova azungulira anthu ake kuyambira tsopano mpaka muyaya.
Горы окрест его, и Господь окрест людий Своих, отныне и до века.
3 Ndodo yaufumu ya anthu oyipa sidzakhala pa dziko limene lapatsidwa kwa anthu olungama, kuti anthu olungamawo angachite nawonso zoyipa.
Яко не оставит Господь жезла грешных на жребий праведных, яко да не прострут праведнии в беззакония рук своих.
4 Yehova chitirani zabwino amene ndi abwino, amene ndi olungama mtima
Ублажи, Господи, благия и правыя сердцем.
5 Koma amene amatembenukira ku njira zokhotakhota, Yehova adzawachotsa pamodzi ndi anthu ochita zoyipa. Mtendere ukhale pa Israeli.
Уклоняющыяся же в развращения отведет Господь с делающими беззаконие: мир на Израиля.

< Masalimo 125 >