< Masalimo 125 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Amene amadalira Yehova ali ngati phiri la Ziyoni, limene silingagwedezeke koma ndi lokhala mpaka muyaya.
Cantique de Maaloth. Ceux qui se confient en l'Éternel sont comme la montagne de Sion, qui ne peut être ébranlée, et qui subsiste à toujours.
2 Monga mapiri azungulira Yerusalemu, momwemonso Yehova azungulira anthu ake kuyambira tsopano mpaka muyaya.
Jérusalem est environnée de montagnes; et l'Éternel est autour de son peuple, dès maintenant et à toujours.
3 Ndodo yaufumu ya anthu oyipa sidzakhala pa dziko limene lapatsidwa kwa anthu olungama, kuti anthu olungamawo angachite nawonso zoyipa.
Car le sceptre de la méchanceté ne reposera pas sur le lot des justes; de peur que les justes ne mettent leurs mains à l'iniquité.
4 Yehova chitirani zabwino amene ndi abwino, amene ndi olungama mtima
Éternel, fais du bien aux bons, à ceux qui ont le cœur droit!
5 Koma amene amatembenukira ku njira zokhotakhota, Yehova adzawachotsa pamodzi ndi anthu ochita zoyipa. Mtendere ukhale pa Israeli.
Mais pour ceux qui se détournent dans des voies tortueuses, l'Éternel les fera marcher avec les ouvriers d'iniquité. Que la paix soit sur Israël!

< Masalimo 125 >