< Masalimo 125 >
1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Amene amadalira Yehova ali ngati phiri la Ziyoni, limene silingagwedezeke koma ndi lokhala mpaka muyaya.
Cantique de Mahaloth. Ceux qui se confient en l'Eternel sont comme la montagne de Sion, qui ne peut être ébranlée, et qui se soutient à toujours.
2 Monga mapiri azungulira Yerusalemu, momwemonso Yehova azungulira anthu ake kuyambira tsopano mpaka muyaya.
Quant à Jérusalem, il y a des montagnes à l'entour d'elle, et l'Eternel est à l'entour de son peuple, dès maintenant et à toujours.
3 Ndodo yaufumu ya anthu oyipa sidzakhala pa dziko limene lapatsidwa kwa anthu olungama, kuti anthu olungamawo angachite nawonso zoyipa.
Car la verge de la méchanceté ne reposera point sur le lot des justes; de peur que les justes ne mettent leurs mains à l'iniquité.
4 Yehova chitirani zabwino amene ndi abwino, amene ndi olungama mtima
Eternel, bénis les gens de bien et ceux dont le cœur est droit.
5 Koma amene amatembenukira ku njira zokhotakhota, Yehova adzawachotsa pamodzi ndi anthu ochita zoyipa. Mtendere ukhale pa Israeli.
Mais quant à ceux qui tordent leurs sentiers obliques, l'Eternel les fera marcher avec les ouvriers d'iniquité. La paix [sera] sur Israël.