< Masalimo 125 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Amene amadalira Yehova ali ngati phiri la Ziyoni, limene silingagwedezeke koma ndi lokhala mpaka muyaya.
Cantique des degrés. Ceux qui ont confiance en l’Eternel seront comme la montagne de Sion, qui ne chancelle pas, inébranlable à jamais.
2 Monga mapiri azungulira Yerusalemu, momwemonso Yehova azungulira anthu ake kuyambira tsopano mpaka muyaya.
Jérusalem a des montagnes pour ceinture; ainsi l’Eternel entoure son peuple, maintenant et pour toujours.
3 Ndodo yaufumu ya anthu oyipa sidzakhala pa dziko limene lapatsidwa kwa anthu olungama, kuti anthu olungamawo angachite nawonso zoyipa.
Car le sceptre de l’impiété ne se posera pas sur le patrimoine des justes, pour que les justes n’appliquent pas leurs mains au mal.
4 Yehova chitirani zabwino amene ndi abwino, amene ndi olungama mtima
Seigneur, fais du bien aux bons, à ceux qui ont le cœur droit.
5 Koma amene amatembenukira ku njira zokhotakhota, Yehova adzawachotsa pamodzi ndi anthu ochita zoyipa. Mtendere ukhale pa Israeli.
Mais ceux qui se détournent vers des voies obliques, que l’Eternel les entraîne avec les artisans d’iniquité! Paix sur Israël!

< Masalimo 125 >