< Masalimo 125 >
1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Amene amadalira Yehova ali ngati phiri la Ziyoni, limene silingagwedezeke koma ndi lokhala mpaka muyaya.
[A Song of Ascents.] Those who trust in YHWH are as Mount Zion, which cannot be moved, but remains forever.
2 Monga mapiri azungulira Yerusalemu, momwemonso Yehova azungulira anthu ake kuyambira tsopano mpaka muyaya.
As the mountains surround Jerusalem, so YHWH surrounds his people from this time forth and forevermore.
3 Ndodo yaufumu ya anthu oyipa sidzakhala pa dziko limene lapatsidwa kwa anthu olungama, kuti anthu olungamawo angachite nawonso zoyipa.
For the scepter of wickedness won't remain over the allotment of the righteous; so that the righteous won't use their hands to do evil.
4 Yehova chitirani zabwino amene ndi abwino, amene ndi olungama mtima
Do good, YHWH, to those who are good, to those who are upright in their hearts.
5 Koma amene amatembenukira ku njira zokhotakhota, Yehova adzawachotsa pamodzi ndi anthu ochita zoyipa. Mtendere ukhale pa Israeli.
But as for those who turn aside to their crooked ways, YHWH will lead them away with evildoers. Peace be on Israel.