< Masalimo 125 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Amene amadalira Yehova ali ngati phiri la Ziyoni, limene silingagwedezeke koma ndi lokhala mpaka muyaya.
Píseň stupňů. Ti, kteříž doufají v Hospodina, podobni jsou k hoře Sionu, kteráž se nepohybuje, ale na věky zůstává.
2 Monga mapiri azungulira Yerusalemu, momwemonso Yehova azungulira anthu ake kuyambira tsopano mpaka muyaya.
Okolo Jeruzaléma jsou hory, Hospodin jest vůkol lidu svého, od tohoto času až na věky.
3 Ndodo yaufumu ya anthu oyipa sidzakhala pa dziko limene lapatsidwa kwa anthu olungama, kuti anthu olungamawo angachite nawonso zoyipa.
Neboť nebude státi sceptrum bezbožníků nad losem spravedlivých, aby nevztáhli spravedliví k nepravosti rukou svých.
4 Yehova chitirani zabwino amene ndi abwino, amene ndi olungama mtima
Dobře učiň, Hospodine, dobrým, a těm, kteříž jsou upřímého srdce.
5 Koma amene amatembenukira ku njira zokhotakhota, Yehova adzawachotsa pamodzi ndi anthu ochita zoyipa. Mtendere ukhale pa Israeli.
Ty pak, kteříž se uchylují k cestám svým křivým, zapudiž Hospodin s činiteli nepravosti. Pokoj přijdiž na Izraele.

< Masalimo 125 >