< Masalimo 125 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Amene amadalira Yehova ali ngati phiri la Ziyoni, limene silingagwedezeke koma ndi lokhala mpaka muyaya.
Песен на възкачванията. Ония, които уповават на Господа, Са като хълма Сион, който не може да се поклати, А до века остава.
2 Monga mapiri azungulira Yerusalemu, momwemonso Yehova azungulira anthu ake kuyambira tsopano mpaka muyaya.
Както хълмовете окръжават Ерусалим, Така Господ окръжава людете Си От сега и до века.
3 Ndodo yaufumu ya anthu oyipa sidzakhala pa dziko limene lapatsidwa kwa anthu olungama, kuti anthu olungamawo angachite nawonso zoyipa.
Защото нечестието няма да налага скиптъра си върху участта на праведните, Да не би праведните да простират ръце към беззаконието.
4 Yehova chitirani zabwino amene ndi abwino, amene ndi olungama mtima
Стори добро, Господи, на добрите И на праведните в сърце.
5 Koma amene amatembenukira ku njira zokhotakhota, Yehova adzawachotsa pamodzi ndi anthu ochita zoyipa. Mtendere ukhale pa Israeli.
А на ония, които се отклоняват в кривите си пътища, Тях ще отведе Господ заедно с ония, които вършат беззаконие. Мир на Израиля!

< Masalimo 125 >