< Masalimo 124 >

1 Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Akanapanda kukhala mbali yathu Yehova, anene tsono Israeli,
A Song of Ascents; of David. 'If it had not been the LORD who was for us', let Israel now say;
2 akanapanda kukhala mbali yathu Yehova, potiwukira anthuwo,
'If it had not been the LORD who was for us, when men rose up against us,
3 iwo atatipsera mtima, akanatimeza amoyo;
Then they had swallowed us up alive, when their wrath was kindled against us;
4 chigumula chikanatimiza, mtsinje ukanatikokolola,
Then the waters had overwhelmed us, the stream had gone over our soul;
5 madzi a mkokomo akanatikokolola.
Then the proud waters had gone over our soul.'
6 Atamandike Yehova, amene sanalole kuti tikhale chakudya cha mano awo.
Blessed be the LORD, who hath not given us as a prey to their teeth.
7 Moyo wathu wawonjoka ngati mbalame yokodwa mu msampha wa mlenje; msampha wathyoka, ndipo ife tapulumuka.
Our soul is escaped as a bird out of the snare of the fowlers; the snare is broken, and we are escaped.
8 Thandizo lathu lili mʼdzina la Yehova wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
Our help is in the name of the LORD, who made heaven and earth.

< Masalimo 124 >