< Masalimo 122 >
1 Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndinakondwera atandiwuza kuti, “Tiyeni ku nyumba ya Yehova.”
En sang ved festreisene; av David. Jeg gleder mig ved dem som sier til mig: Vi vil gå til Herrens hus.
2 Mapazi athu akuyima mʼzipata zako, Iwe Yerusalemu.
Våre føtter står i dine porter, Jerusalem!
3 Yerusalemu anamangidwa ngati mzinda umene uli wothithikana pamodzi.
Jerusalem, du velbyggede, lik en by som er tett sammenføiet,
4 Kumeneko ndiye kumene kumapita mafuko, mafuko a Yehova, umboni wa kwa Israeli, kuti atamande dzina la Yehova.
hvor stammene drar op, Herrens stammer, efter en lov for Israel, for å prise Herrens navn!
5 Kumeneko anayikako mipando yaufumu yachiweruzo, mipando yaufumu ya nyumba ya Davide.
For der er stoler satt til dom, stoler for Davids hus.
6 Pemphererani mtendere wa Yerusalemu: “Iwo amene amakukonda iwe zinthu ziwayendere bwino.
Bed om fred for Jerusalem! La det gå dem vel som elsker dig!
7 Mukhale mtendere mʼkati mwa makoma ako, ndipo mʼnyumba zako zaufumu mukhale chitetezo.”
Der være fred innen din voll, ro i dine saler!
8 Chifukwa cha abale anga ndi abwenzi anga ndidzati, “Mtendere ukhale mʼkati mwako.”
For mine brødres og mine venners skyld vil jeg si: Fred være i dig!
9 Chifukwa cha Nyumba ya Yehova Mulungu wathu, ndidzakufunira zabwino.
For Herrens, vår Guds huses skyld vil jeg søke ditt beste.