< Masalimo 122 >

1 Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndinakondwera atandiwuza kuti, “Tiyeni ku nyumba ya Yehova.”
Ingoma yemiqanso. ElikaDavida. Ngathokoza lalabo abathi kimi, “Kasiye endlini kaThixo.”
2 Mapazi athu akuyima mʼzipata zako, Iwe Yerusalemu.
Inyawo zethu zimi ngaphakathi kwamasango akho, wena Jerusalema.
3 Yerusalemu anamangidwa ngati mzinda umene uli wothithikana pamodzi.
IJerusalema yakhiwe njengomuzi obambeneyo waqina.
4 Kumeneko ndiye kumene kumapita mafuko, mafuko a Yehova, umboni wa kwa Israeli, kuti atamande dzina la Yehova.
Kulapho eziqansela khona izizwana, izizwana zikaThixo, ukudumisa ibizo likaThixo njengalokho okwamiselwa u-Israyeli, ukuba abonge ibizo likaThixo.
5 Kumeneko anayikako mipando yaufumu yachiweruzo, mipando yaufumu ya nyumba ya Davide.
Kulapho okumi khona izihlalo zobukhosi ezokwahlulela, izihlalo zobukhosi ezendlu kaDavida.
6 Pemphererani mtendere wa Yerusalemu: “Iwo amene amakukonda iwe zinthu ziwayendere bwino.
Khulekelani ukuthula kwaseJerusalema: “Sengathi labo abakuthandayo bangaphepha.
7 Mukhale mtendere mʼkati mwa makoma ako, ndipo mʼnyumba zako zaufumu mukhale chitetezo.”
Sengathi kungaba lokuthula ngaphakathi kwemiduli yakho lokuvikela ngaphakathi kwezinqaba zakho.”
8 Chifukwa cha abale anga ndi abwenzi anga ndidzati, “Mtendere ukhale mʼkati mwako.”
Ngenxa yabafowethu labangane bami, ngizakuthi, “Ukuthula akube ngaphakathi kwakho.”
9 Chifukwa cha Nyumba ya Yehova Mulungu wathu, ndidzakufunira zabwino.
Ngenxa yendlu kaThixo uNkulunkulu wethu, ngizakhuthaza ukuphumelela kwakho.

< Masalimo 122 >