< Masalimo 122 >
1 Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndinakondwera atandiwuza kuti, “Tiyeni ku nyumba ya Yehova.”
Ich bin froh, wenn sie zu mir sagen: Lasset uns gehen nach dem Hause Jehovahs!
2 Mapazi athu akuyima mʼzipata zako, Iwe Yerusalemu.
In deinen Toren stehen unsere Füße, o Jerusalem.
3 Yerusalemu anamangidwa ngati mzinda umene uli wothithikana pamodzi.
Jerusalem, die gebaut ist wie eine Stadt, die für sich zusammengefügt ist in eins.
4 Kumeneko ndiye kumene kumapita mafuko, mafuko a Yehova, umboni wa kwa Israeli, kuti atamande dzina la Yehova.
Wo hinaufziehen die Stämme, die Stämme Jahs, ein Zeugnis für Israel, zu bekennen den Namen Jehovahs.
5 Kumeneko anayikako mipando yaufumu yachiweruzo, mipando yaufumu ya nyumba ya Davide.
Denn dort sitzen Throne zum Gericht, Throne von Davids Haus.
6 Pemphererani mtendere wa Yerusalemu: “Iwo amene amakukonda iwe zinthu ziwayendere bwino.
Bittet um den Frieden Jerusalems. In Ruhe seien, die dich lieben.
7 Mukhale mtendere mʼkati mwa makoma ako, ndipo mʼnyumba zako zaufumu mukhale chitetezo.”
Friede sei in deiner Vormauer, Ruhe in deinen Palästen!
8 Chifukwa cha abale anga ndi abwenzi anga ndidzati, “Mtendere ukhale mʼkati mwako.”
Um meiner Brüder und Genossen willen laß mich doch reden: Friede sei in dir!
9 Chifukwa cha Nyumba ya Yehova Mulungu wathu, ndidzakufunira zabwino.
Um des Hauses Jehovahs unseres Gottes willen will ich dir Gutes suchen.