< Masalimo 122 >
1 Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndinakondwera atandiwuza kuti, “Tiyeni ku nyumba ya Yehova.”
Ein Stufenlied von David. / Ich hab mich gefreut über die, die zu mir sagten: / "Zu Jahwes Hause wollen wir wallen."
2 Mapazi athu akuyima mʼzipata zako, Iwe Yerusalemu.
Dann standen endlich unsre Füße / In deinen Toren, Jerusalem.
3 Yerusalemu anamangidwa ngati mzinda umene uli wothithikana pamodzi.
Jerusalem, du wiedererbaute, / Als eine Stadt, die eng in sich verbunden!
4 Kumeneko ndiye kumene kumapita mafuko, mafuko a Yehova, umboni wa kwa Israeli, kuti atamande dzina la Yehova.
Dorthin zogen die Stämme hinauf, / Die Stämme Jahs — / Wie es Israel vorgeschrieben —, / Um Jahwes Namen zu preisen.
5 Kumeneko anayikako mipando yaufumu yachiweruzo, mipando yaufumu ya nyumba ya Davide.
Dort standen einst die Stühle für die Gerichtsverhandlung, / Stühle für Davids Haus.
6 Pemphererani mtendere wa Yerusalemu: “Iwo amene amakukonda iwe zinthu ziwayendere bwino.
Erbittet Jerusalem Frieden! / Wohl geh es denen, die dich lieben!
7 Mukhale mtendere mʼkati mwa makoma ako, ndipo mʼnyumba zako zaufumu mukhale chitetezo.”
Friede walte in deinen Mauern, / Sicherheit in deinen Palästen!
8 Chifukwa cha abale anga ndi abwenzi anga ndidzati, “Mtendere ukhale mʼkati mwako.”
Um meiner Brüder und Freunde willen / Will ich doch sagen: "Friede walte in dir!"
9 Chifukwa cha Nyumba ya Yehova Mulungu wathu, ndidzakufunira zabwino.
Aus Liebe zum Hause Jahwes, unsers Gottes, / Will ich dein Bestes suchen.