< Masalimo 122 >
1 Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndinakondwera atandiwuza kuti, “Tiyeni ku nyumba ya Yehova.”
Cantique des degrés. Je me suis réjoui des paroles qui m’ont été dites: Nous irons dans la maison du Seigneur.
2 Mapazi athu akuyima mʼzipata zako, Iwe Yerusalemu.
Nos pieds se tenaient dans tes parvis, ô Jérusalem.
3 Yerusalemu anamangidwa ngati mzinda umene uli wothithikana pamodzi.
Jérusalem, que l’on bâtit comme une cité dont les parties sont unies ensemble.
4 Kumeneko ndiye kumene kumapita mafuko, mafuko a Yehova, umboni wa kwa Israeli, kuti atamande dzina la Yehova.
Car, là sont montées les tribus, les tribus du Seigneur; témoignage d’Israël, pour y louer le nom du Seigneur.
5 Kumeneko anayikako mipando yaufumu yachiweruzo, mipando yaufumu ya nyumba ya Davide.
Parce que là ont été établis des tribunaux pour le jugement, des trônes pour la maison de David.
6 Pemphererani mtendere wa Yerusalemu: “Iwo amene amakukonda iwe zinthu ziwayendere bwino.
Demandez ce qui importe à la paix de Jérusalem: et que l’abondance soit à ceux qui t’aiment, ô cité sainte.
7 Mukhale mtendere mʼkati mwa makoma ako, ndipo mʼnyumba zako zaufumu mukhale chitetezo.”
Que la paix règne dans ta force, et l’abondance dans tes tours.
8 Chifukwa cha abale anga ndi abwenzi anga ndidzati, “Mtendere ukhale mʼkati mwako.”
À cause de mes frères et de mes proches, je parlais paix à ton sujet;
9 Chifukwa cha Nyumba ya Yehova Mulungu wathu, ndidzakufunira zabwino.
À cause de la maison du Seigneur notre Dieu, j’ai cherché des biens pour toi.