< Masalimo 122 >

1 Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndinakondwera atandiwuza kuti, “Tiyeni ku nyumba ya Yehova.”
A song of ascents, of David. I was glad when they said to me, “Let us go to the house of Yahweh.”
2 Mapazi athu akuyima mʼzipata zako, Iwe Yerusalemu.
Jerusalem, our feet are standing within your gates!
3 Yerusalemu anamangidwa ngati mzinda umene uli wothithikana pamodzi.
Jerusalem, built as a city carefully planned!
4 Kumeneko ndiye kumene kumapita mafuko, mafuko a Yehova, umboni wa kwa Israeli, kuti atamande dzina la Yehova.
The tribes go up to Jerusalem—the tribes of Yahweh— as a testimony for Israel, to give thanks to the name of Yahweh.
5 Kumeneko anayikako mipando yaufumu yachiweruzo, mipando yaufumu ya nyumba ya Davide.
There thrones of judgment were set, thrones of the house of David.
6 Pemphererani mtendere wa Yerusalemu: “Iwo amene amakukonda iwe zinthu ziwayendere bwino.
Pray for the peace of Jerusalem! “May those who love you have peace.
7 Mukhale mtendere mʼkati mwa makoma ako, ndipo mʼnyumba zako zaufumu mukhale chitetezo.”
May there be peace within the walls that defend you, and may they have peace within your fortresses.”
8 Chifukwa cha abale anga ndi abwenzi anga ndidzati, “Mtendere ukhale mʼkati mwako.”
For the sake of my brothers and my friends I will say, “May there be peace within you.”
9 Chifukwa cha Nyumba ya Yehova Mulungu wathu, ndidzakufunira zabwino.
For the sake of the house of Yahweh our God, I will seek good for you.

< Masalimo 122 >