< Masalimo 122 >

1 Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndinakondwera atandiwuza kuti, “Tiyeni ku nyumba ya Yehova.”
I was glad/happy when people said to me, “We should go to the temple of Yahweh [in Jerusalem]!”
2 Mapazi athu akuyima mʼzipata zako, Iwe Yerusalemu.
And now we are here, standing inside the gates/city of [APO] Jerusalem.
3 Yerusalemu anamangidwa ngati mzinda umene uli wothithikana pamodzi.
Jerusalem is a city that has been rebuilt, with the result that people can gather together in it.
4 Kumeneko ndiye kumene kumapita mafuko, mafuko a Yehova, umboni wa kwa Israeli, kuti atamande dzina la Yehova.
We [people of the] tribes of Israel who belong to Yahweh can now go up there as Yahweh commanded that we should do, and we can thank him.
5 Kumeneko anayikako mipando yaufumu yachiweruzo, mipando yaufumu ya nyumba ya Davide.
There the kings of Israel who were descendants of [King] David sit on their thrones and decide cases [fairly when the people have disputes].
6 Pemphererani mtendere wa Yerusalemu: “Iwo amene amakukonda iwe zinthu ziwayendere bwino.
Pray that there will be peace in Jerusalem; I desire that those who love Jerusalem will (prosper/live peacefully).
7 Mukhale mtendere mʼkati mwa makoma ako, ndipo mʼnyumba zako zaufumu mukhale chitetezo.”
I desire that there will be peace inside the walls of the city and that [people who are] inside the palaces will be safe.
8 Chifukwa cha abale anga ndi abwenzi anga ndidzati, “Mtendere ukhale mʼkati mwako.”
For the sake of my relatives and friends, I say, “My desire is that that inside Jerusalem [people will live] peacefully.”
9 Chifukwa cha Nyumba ya Yehova Mulungu wathu, ndidzakufunira zabwino.
And because I love the temple of Yahweh our God, I pray that things will go well for the people who live [in Jerusalem].

< Masalimo 122 >