< Masalimo 122 >
1 Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndinakondwera atandiwuza kuti, “Tiyeni ku nyumba ya Yehova.”
A song of ascents. Of David. I was glad when they said to me, “We will go to the house of the Lord.”
2 Mapazi athu akuyima mʼzipata zako, Iwe Yerusalemu.
Now we are standing, within your gates, O Jerusalem.
3 Yerusalemu anamangidwa ngati mzinda umene uli wothithikana pamodzi.
O Jerusalem, built close-packed, like a city without breach or gap,
4 Kumeneko ndiye kumene kumapita mafuko, mafuko a Yehova, umboni wa kwa Israeli, kuti atamande dzina la Yehova.
to you do the tribes come, the tribes of the Lord, as the law has ordained for Israel, there to give thanks to the Lord.
5 Kumeneko anayikako mipando yaufumu yachiweruzo, mipando yaufumu ya nyumba ya Davide.
There once stood thrones of justice even thrones of the household of David.
6 Pemphererani mtendere wa Yerusalemu: “Iwo amene amakukonda iwe zinthu ziwayendere bwino.
Pray that all may be well with Jerusalem, and well with those who love you,
7 Mukhale mtendere mʼkati mwa makoma ako, ndipo mʼnyumba zako zaufumu mukhale chitetezo.”
well within your ramparts, and well within your palaces.
8 Chifukwa cha abale anga ndi abwenzi anga ndidzati, “Mtendere ukhale mʼkati mwako.”
For the sake of my brethren and friends, I will wish you now prosperity:
9 Chifukwa cha Nyumba ya Yehova Mulungu wathu, ndidzakufunira zabwino.
for the sake of the house of the Lord our God, I will seek your good.