< Masalimo 122 >

1 Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndinakondwera atandiwuza kuti, “Tiyeni ku nyumba ya Yehova.”
“A psalm of the steps, or the goings up. By David.” I was glad when they said to me, Let us go up to the house of the LORD!
2 Mapazi athu akuyima mʼzipata zako, Iwe Yerusalemu.
Our feet are standing Within thy gates, O Jerusalem!
3 Yerusalemu anamangidwa ngati mzinda umene uli wothithikana pamodzi.
Jerusalem, the rebuilt city! The city that is joined together!
4 Kumeneko ndiye kumene kumapita mafuko, mafuko a Yehova, umboni wa kwa Israeli, kuti atamande dzina la Yehova.
Thither the tribes go up, The tribes of the LORD, according to the law of Israel, To praise the name of the LORD.
5 Kumeneko anayikako mipando yaufumu yachiweruzo, mipando yaufumu ya nyumba ya Davide.
There stand the thrones of judgment, The thrones of the house of David.
6 Pemphererani mtendere wa Yerusalemu: “Iwo amene amakukonda iwe zinthu ziwayendere bwino.
Pray for the peace of Jerusalem! May they prosper who love thee!
7 Mukhale mtendere mʼkati mwa makoma ako, ndipo mʼnyumba zako zaufumu mukhale chitetezo.”
Peace be within thy walls, And prosperity within thy palaces!
8 Chifukwa cha abale anga ndi abwenzi anga ndidzati, “Mtendere ukhale mʼkati mwako.”
For my brethren and companions' sake will I say, Peace be within thee!
9 Chifukwa cha Nyumba ya Yehova Mulungu wathu, ndidzakufunira zabwino.
For the sake of the house of the LORD, our God, Will I seek thy good!

< Masalimo 122 >