< Masalimo 122 >
1 Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndinakondwera atandiwuza kuti, “Tiyeni ku nyumba ya Yehova.”
Píseň stupňů, Davidova. Veselím se z toho, že mi říkáno bývá: Poďme do domu Hospodinova,
2 Mapazi athu akuyima mʼzipata zako, Iwe Yerusalemu.
A že se postavují nohy naše v branách tvých, ó Jeruzaléme.
3 Yerusalemu anamangidwa ngati mzinda umene uli wothithikana pamodzi.
Jižtě Jeruzalém ušlechtile vystaven, a jako v město k sobě vespolek připojen.
4 Kumeneko ndiye kumene kumapita mafuko, mafuko a Yehova, umboni wa kwa Israeli, kuti atamande dzina la Yehova.
Do něhož vstupují pokolení, pokolení Hospodinova, k svědectví Izraelovu, aby oslavovali jméno Hospodinovo.
5 Kumeneko anayikako mipando yaufumu yachiweruzo, mipando yaufumu ya nyumba ya Davide.
Nebo tamť jsou postaveny stolice soudu, stolice domu Davidova.
6 Pemphererani mtendere wa Yerusalemu: “Iwo amene amakukonda iwe zinthu ziwayendere bwino.
Žádejtež pokoje Jeruzalému, řkouce: Dějž se pokojně těm, kteříž tě milují.
7 Mukhale mtendere mʼkati mwa makoma ako, ndipo mʼnyumba zako zaufumu mukhale chitetezo.”
Budiž pokoj v předhradí tvém, a upokojení na palácích tvých.
8 Chifukwa cha abale anga ndi abwenzi anga ndidzati, “Mtendere ukhale mʼkati mwako.”
Pro bratří své a přátely své žádati budu pokoje tobě.
9 Chifukwa cha Nyumba ya Yehova Mulungu wathu, ndidzakufunira zabwino.
Pro dům Hospodina Boha našeho budu tvého dobrého hledati.