< Masalimo 121 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndikweza maso anga ku mapiri; kodi thandizo langa limachokera kuti?
Ɔsoroforɔ dwom. Mema mʼani so kyerɛ mmepɔ no, ɛhe na me mmoa firi bɛba?
2 Thandizo langa limachokera kwa Yehova, wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
Me mmoa firi Awurade, ɔsoro ne asase yɛfoɔ no.
3 Sadzalola kuti phazi lako literereke; Iye amene amakusunga sadzawodzera.
Ɔremma wo nan nwatiri, deɛ ɔhwɛ wo no, ɔrentɔ nko.
4 Taonani, Iye amene amasunga Israeli sadzawodzera kapena kugona.
Ampa ara deɛ ɔhwɛ Israel no rentɔ nko na ɔrenna.
5 Yehova ndiye amene amakusunga; Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.
Awurade hwɛ wo so; Awurade ne wo nwunu wɔ wo nsa nifa so;
6 Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana, kapena mwezi nthawi ya usiku.
Owia renhye wo wɔ awiaberɛ mu, na ɔsrane nso renha wo anadwo.
7 Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse; adzasunga moyo wako.
Awurade bɛbɔ wo ho ban afiri ɔhaw nyinaa ho, ɔbɛhwɛ wo nkwa so;
8 Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako; kuyambira tsopano mpaka muyaya.
Awurade bɛhwɛ wʼadifire ne wo efieba so, seesei ne daa.

< Masalimo 121 >