< Masalimo 121 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndikweza maso anga ku mapiri; kodi thandizo langa limachokera kuti?
われ山にむかひて目をあぐ わが扶助はいづこよりきたるや
2 Thandizo langa limachokera kwa Yehova, wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
わがたすけは天地をつくりたまへるヱホバよりきたる
3 Sadzalola kuti phazi lako literereke; Iye amene amakusunga sadzawodzera.
ヱホバはなんぢの足のうごかさるるを容したまはず 汝をまもるものは微睡たまふことなし
4 Taonani, Iye amene amasunga Israeli sadzawodzera kapena kugona.
視よイスラエルを守りたまふものは微睡こともなく寝ることもなからん
5 Yehova ndiye amene amakusunga; Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.
ヱホバは汝をまもる者なり ヱホバはなんぢの右手をおほふ蔭なり
6 Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana, kapena mwezi nthawi ya usiku.
ひるは日なんぢをうたず夜は月なんぢを傷じ
7 Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse; adzasunga moyo wako.
ヱホバはなんぢを守りてもろもろの禍害をまぬかれしめ並なんぢの霊魂をまもりたまはん
8 Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako; kuyambira tsopano mpaka muyaya.
ヱホバは今よりとこしへにいたるまで 汝のいづると入るとをまもりたまはん

< Masalimo 121 >