< Masalimo 121 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndikweza maso anga ku mapiri; kodi thandizo langa limachokera kuti?
שיר למעלות אשא עיני אל-ההרים-- מאין יבא עזרי
2 Thandizo langa limachokera kwa Yehova, wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
עזרי מעם יהוה-- עשה שמים וארץ
3 Sadzalola kuti phazi lako literereke; Iye amene amakusunga sadzawodzera.
אל-יתן למוט רגלך אל-ינום שמרך
4 Taonani, Iye amene amasunga Israeli sadzawodzera kapena kugona.
הנה לא-ינום ולא יישן-- שומר ישראל
5 Yehova ndiye amene amakusunga; Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.
יהוה שמרך יהוה צלך על-יד ימינך
6 Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana, kapena mwezi nthawi ya usiku.
יומם השמש לא-יככה וירח בלילה
7 Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse; adzasunga moyo wako.
יהוה ישמרך מכל-רע ישמר את-נפשך
8 Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako; kuyambira tsopano mpaka muyaya.
יהוה ישמר-צאתך ובואך-- מעתה ועד-עולם

< Masalimo 121 >