< Masalimo 121 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndikweza maso anga ku mapiri; kodi thandizo langa limachokera kuti?
J’ai levé les yeux vers les montagnes, d’où me viendra le secours.
2 Thandizo langa limachokera kwa Yehova, wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
Mon secours vient du Seigneur, qui a fait le ciel et la terre.
3 Sadzalola kuti phazi lako literereke; Iye amene amakusunga sadzawodzera.
Qu’il ne permette pas que ton pied soit ébranlé, et qu’il ne s’assoupisse pas, celui qui te garde.
4 Taonani, Iye amene amasunga Israeli sadzawodzera kapena kugona.
Vois, il ne s’assoupira, ni ne dormira, celui qui garde Israël.
5 Yehova ndiye amene amakusunga; Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.
C’est le Seigneur qui te garde, c’est le Seigneur qui est ta protection; il est sur ta main droite.
6 Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana, kapena mwezi nthawi ya usiku.
Pendant le jour, le soleil ne le brûlera pas, ni la lune pendant la nuit.
7 Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse; adzasunga moyo wako.
Le Seigneur te garde de tout mal; que le Seigneur garde ton âme.
8 Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako; kuyambira tsopano mpaka muyaya.
Que le Seigneur garde ton entrée et ta sortie, dès ce moment et jusqu’à jamais.

< Masalimo 121 >