< Masalimo 121 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndikweza maso anga ku mapiri; kodi thandizo langa limachokera kuti?
I have lifted up my eyes to the mountains, from whence help shall come to me.
2 Thandizo langa limachokera kwa Yehova, wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
My help is from the Lord, who made heaven and earth.
3 Sadzalola kuti phazi lako literereke; Iye amene amakusunga sadzawodzera.
May he not suffer thy foot to be moved: neither let him slumber that keepeth thee.
4 Taonani, Iye amene amasunga Israeli sadzawodzera kapena kugona.
Behold he shall neither slumber nor sleep, that keepeth Israel.
5 Yehova ndiye amene amakusunga; Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.
The Lord is thy keeper, the Lord is thy protection upon thy right hand.
6 Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana, kapena mwezi nthawi ya usiku.
The sun shall not burn thee by day: nor the moon by night.
7 Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse; adzasunga moyo wako.
The Lord keepeth thee from all evil: may the Lord keep thy soul.
8 Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako; kuyambira tsopano mpaka muyaya.
May the Lord keep thy going in and thy going out; from henceforth now and for ever.

< Masalimo 121 >