< Masalimo 121 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndikweza maso anga ku mapiri; kodi thandizo langa limachokera kuti?
I will lift up my eyes to the mountains. From where shall my help come?
2 Thandizo langa limachokera kwa Yehova, wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
My help is from Jehovah, who made heaven and earth.
3 Sadzalola kuti phazi lako literereke; Iye amene amakusunga sadzawodzera.
He will not allow thy foot to be moved. He who keeps thee will not slumber.
4 Taonani, Iye amene amasunga Israeli sadzawodzera kapena kugona.
Behold, he who keeps Israel will neither slumber nor sleep.
5 Yehova ndiye amene amakusunga; Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.
Jehovah is thy keeper. Jehovah is thy shade upon thy right hand.
6 Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana, kapena mwezi nthawi ya usiku.
The sun shall not smite thee by day, nor the moon by night.
7 Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse; adzasunga moyo wako.
Jehovah will keep thee from all evil. He will keep thy soul.
8 Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako; kuyambira tsopano mpaka muyaya.
Jehovah will keep thy going out and thy coming in from this time forth and for evermore.

< Masalimo 121 >