< Masalimo 120 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga, ndipo Iye amandiyankha.
Кэтре Домнул стриг ын стрымтораря мя, ши Ел м-аскултэ.
2 Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza, ndi kwa anthu achinyengo.
Доамне, скапэ-мь суфлетул де буза минчиноасэ, де лимба ыншелэтоаре!
3 Kodi adzakuchitani chiyani, ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo?
Че-ць дэ Ел цие, че-ць адуче Ел цие, лимбэ ыншелэтоаре?
4 Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo, ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya.
Сэӂець аскуците де рэзбойник, ку кэрбунь априншь де енупэр.
5 Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki, kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara!
Вай де мине кэ локуеск ла Мешек, кэ локуеск ын кортуриле Кедарулуй!
6 Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati pa iwo amene amadana ndi mtendere.
Дестул мь-а локуит суфлетул лынгэ чей че урэск пачя.
7 Ine ndine munthu wamtendere; koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.
Еу сунт пентру паче, дар де ындатэ че ворбеск еу, ей сунт пентру рэзбой.

< Masalimo 120 >