< Masalimo 120 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga, ndipo Iye amandiyankha.
Na minha angustia clamei ao Senhor, e me ouviu.
2 Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza, ndi kwa anthu achinyengo.
Senhor, livra a minha alma dos labios mentirosos e da lingua enganadora.
3 Kodi adzakuchitani chiyani, ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo?
Que te será dado, ou que te será accrescentado, lingua enganadora?
4 Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo, ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya.
Frechas agudas do valente, com brazas vivas de zimbro.
5 Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki, kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara!
Ai de mim, que peregrino em Mesech, e habito nas tendas de Kedar.
6 Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati pa iwo amene amadana ndi mtendere.
A minha alma bastante tempo habitou com os que detestam a paz.
7 Ine ndine munthu wamtendere; koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.
Pacifico sou, porém quando eu fallo já elles procuram guerra.

< Masalimo 120 >