< Masalimo 120 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga, ndipo Iye amandiyankha.
Oluyimba nga balinnya amadaala. Nkoowoola Mukama nga ndi mu nnaku, era n’annyanukula.
2 Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza, ndi kwa anthu achinyengo.
Omponye, Ayi Mukama, emimwa egy’obulimba, n’olulimi olw’obukuusa.
3 Kodi adzakuchitani chiyani, ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo?
Onooweebwa ki, era onookolebwa otya, ggwe olulimi olukuusa?
4 Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo, ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya.
Onoofumitibwa n’obusaale obwogi obw’omulwanyi omuzira, n’oyokerwa ku manda ag’omuti entaseesa.
5 Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki, kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara!
Ndabye ennaku, kubanga mbeera mu Meseki; nsula mu weema za Kedali!
6 Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati pa iwo amene amadana ndi mtendere.
Ndudde nnyo mu bantu abakyawa eddembe.
7 Ine ndine munthu wamtendere; koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.
Nze njagala mirembe, naye bwe njogera bo baagala ntalo.

< Masalimo 120 >