< Masalimo 120 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga, ndipo Iye amandiyankha.
Zarándoklás éneke. Szorultságomban az Örökkévalóhoz kiáltottam föl és ő meghallgatott engem.
2 Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza, ndi kwa anthu achinyengo.
Örökkévaló, mentsd meg lelkemet hazug ajaktól, csalárdság nyelvétől!
3 Kodi adzakuchitani chiyani, ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo?
Mit ad neked és mit gyarapit neked a csalárdság nyelve?
4 Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo, ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya.
Vitéznek élesített nyilai, meg rekettyének parazsa!
5 Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki, kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara!
Jaj nekem, hogy Mésekhnél tartózkodtam, lakoztam Kédár sátrai mellett!
6 Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati pa iwo amene amadana ndi mtendere.
Sokat lakozott a lelkem a béke gyülölői mellett.
7 Ine ndine munthu wamtendere; koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.
Én merő béke vagyok; de midőn beszélek, ők harczra készek.

< Masalimo 120 >