< Masalimo 120 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga, ndipo Iye amandiyankha.
שיר המעלות אל יהוה בצרתה לי קראתי ויענני׃
2 Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza, ndi kwa anthu achinyengo.
יהוה הצילה נפשי משפת שקר מלשון רמיה׃
3 Kodi adzakuchitani chiyani, ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo?
מה יתן לך ומה יסיף לך לשון רמיה׃
4 Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo, ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya.
חצי גבור שנונים עם גחלי רתמים׃
5 Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki, kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara!
אויה לי כי גרתי משך שכנתי עם אהלי קדר׃
6 Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati pa iwo amene amadana ndi mtendere.
רבת שכנה לה נפשי עם שונא שלום׃
7 Ine ndine munthu wamtendere; koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.
אני שלום וכי אדבר המה למלחמה׃

< Masalimo 120 >