< Masalimo 120 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga, ndipo Iye amandiyankha.
שִׁיר הַֽמַּעֲלוֹת אֶל־יְהֹוָה בַּצָּרָתָה לִּי קָרָאתִי וַֽיַּעֲנֵֽנִי׃
2 Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza, ndi kwa anthu achinyengo.
יְֽהֹוָה הַצִּילָה נַפְשִׁי מִשְּׂפַת־שֶׁקֶר מִלָּשׁוֹן רְמִיָּֽה׃
3 Kodi adzakuchitani chiyani, ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo?
מַה־יִּתֵּן לְךָ וּמַה־יֹּסִיף לָךְ לָשׁוֹן רְמִיָּֽה׃
4 Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo, ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya.
חִצֵּי גִבּוֹר שְׁנוּנִים עִם גַּחֲלֵי רְתָמִֽים׃
5 Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki, kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara!
אֽוֹיָה־לִי כִּי־גַרְתִּי מֶשֶׁךְ שָׁכַנְתִּי עִֽם־אׇהֳלֵי קֵדָֽר׃
6 Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati pa iwo amene amadana ndi mtendere.
רַבַּת שָֽׁכְנָה־לָּהּ נַפְשִׁי עִם שׂוֹנֵא שָׁלֽוֹם׃
7 Ine ndine munthu wamtendere; koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.
אֲֽנִי־שָׁלוֹם וְכִי אֲדַבֵּר הֵמָּה לַמִּלְחָמָֽה׃

< Masalimo 120 >