< Masalimo 120 >
1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga, ndipo Iye amandiyankha.
[Ein Stufenlied.] Zu Jehova rief ich in meiner Bedrängnis, und er erhörte mich.
2 Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza, ndi kwa anthu achinyengo.
Jehova, errette meine Seele von der Lippe der Lüge, von der Zunge des Truges!
3 Kodi adzakuchitani chiyani, ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo?
Was soll man [O. er [Gott]] dir geben und was dir hinzufügen, du Zunge des Truges?
4 Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo, ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya.
Scharfe Pfeile eines Gewaltigen, samt glühenden Kohlen der Ginster.
5 Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki, kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara!
Wehe mir, daß ich weile in Mesech, daß ich wohne bei den Zelten Kedars!
6 Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati pa iwo amene amadana ndi mtendere.
Lange [O. Genug] hat meine Seele bei denen gewohnt, die den Frieden hassen.
7 Ine ndine munthu wamtendere; koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.
Ich will nur Frieden; [W. Ich bin Friede] aber wenn ich rede, so sind sie für Krieg.