< Masalimo 120 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga, ndipo Iye amandiyankha.
Cantique de Maaloth. J'ai crié à l'Éternel dans ma détresse, et il m'a exaucé.
2 Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza, ndi kwa anthu achinyengo.
Éternel, délivre mon âme des lèvres menteuses, de la langue qui trompe!
3 Kodi adzakuchitani chiyani, ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo?
Que te donnera, que te rapportera la langue trompeuse?
4 Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo, ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya.
Des flèches aiguës comme celles du guerrier, avec les charbons ardents du genêt.
5 Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki, kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara!
Malheureux que je suis de séjourner en Méshec, de demeurer parmi les tentes de Kédar!
6 Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati pa iwo amene amadana ndi mtendere.
Trop longtemps mon âme a demeuré avec celui qui hait la paix.
7 Ine ndine munthu wamtendere; koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.
Je veux la paix; mais dès que je parle, ils sont pour la guerre.

< Masalimo 120 >